Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 83

Matigari zinthu zonse za munthu. "Kodi ameneyu si mwana ankalephera kumina yekha uja? Ndi ndani anamupatsa udindo woti agulitse malo athu, mafakitale, nyumba komanso cholowa chathu? Kodi anthu inu munakumana kuti? Ifetu tinkaganiza kuti anthu ophunziranu muima nji polimbana ndi atsamunda omwe amakolola pamene sanalime. Kodi ku Ulaya unapita kuja unkakangosewerako eti? Unayamba bwanji kucheza ndi anthu a mtundu umenewu, om- we amangokhala ngati nthata zoyamwa ena magazi?" Robert Williams ndi John Boy anayamba kunong'onezana. Kenako Williams anamenya hatchi yake n'kunyamuka kumapi- ta. Matigari anayamba kutsegula geti lolowera kunyumba ija. "Tadikirani kaye madala! Popeza mwanena kuti mulibe chikalata chosonyeza kuti nyumbayi ndi yanu, ndiye mwadziwa bwanji kuti ndiyanudi?" anatero John boy. Ankayankhula monyoza zedi, koma Matigari sanamulabade. Chikhumbokhumbo cholowa m'nyumbayo chinali chitamug- wira ndipo chinamukumbutsa zimene zinachitika kale pamene anayamba kulimbana ndi Mtsamunda Williams. Anakumbukira mifuleni yathukuta lomwe anakhetsa, kutopa, mvula, mphepo yomwe inamuumbudza, ululu komanso mavuto onse omwe anakumana nawo. “Tabwera kuno!” anatero Matigari akuyang'ana John Boy m'zikope mwenimweni. Matigari anali ndi khalidwe lapadera. Iye anali ndi mawu aukumu omwe ankachititsa kuti anthu azikopeka naye akamayankhula. Tsopano Matigari ndi John Boy anaima maso ndi maso ngati akupimana mphamvu kuti aone amene ali wanzeru kwambiri. “Tiye kunyumba yanga ndi- kakuonetse makona onse a nyumba imeneyi, komanso ndi- kakuonetse zipinda zonse zomwe ndinazivutikira kuzimanga. 82