Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 81

Matigari nyemba imodzi imene yagwera pansi." "Zodabwitsa sizidzatha padzikoli! Kodi waiwala zimene an- thu anachita posonkherana ndalama kuti akutumize kusukulu? Kapena bambo ako sanakuuze zimenezi? Kodi anthu ophunziranu simukumbukira kuti munaphunzira chifukwa cha anthu omwe mukuwanena kuti zitsiru lerowa? Lero mwasukusula n’kuyamba kuluma dzanja limene linakuthandi- zani! Anthu alibedi pabwino, pabwino anatayira galu." "Kodi munasainirana pati ndi bambo anga kuti ndikubwe- zereni tindalama tomwe mukuti munanditumizira kusukuluto? Ndionetseni kuti ndikubwezereni pompanopompano!" John Boy Junior anayankhula mokuwa ngati kuti akuyankhula pam- sonkhano wandale. "Ndionetsenitu pamene munalemberana! Ndikubwezerani tindalama tanuto, komanso ndiwonjezerepo chiwongoladzanja . . ! Tadikirani ndikuuzeni bambo, zimene zili zanga, ndi zanga. Ngati mukufuna kuti nditenge zinthu zomwe ndi zanu, shauri yanu! Pitani mukatenge zonse mun- dipatse. Ndidzalandira zonse. Mwinanso mungachite bwino kungonyamuka n’kumapita kwanu, ndisanakuonetseni malodza. Kunjaku kwada kale, posachedwapa kunja kukhala kuli chimdima. Sewero lathera pamenepa. Nyamukani mwaulemu muzipita. Panopa nyumbayi ndi ya anthu ena, si ya- nunso bambo, mwamva!" "Wati ndi ya munthu wina? Ikhala bwanji ya wina ngati anamanga ndi iyeyo? Ineyo ndi amene ndinamanga nyumbayi ndipo sindichoka pano." "Mdalayu ndi wamakani ngati wofula agalu. Eti akukakamira kuti nyumbayi ndi yake," wakuda uja anauza Robert Williams. "Tsopano ndithetse malonda amphakawa chifukwa mapeto ake tichedwa kuphwando lokonzekera kubwera kwa nduna ija mawa." 80