Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 74

Matigari kunali nyumba ija ndi dzanja limodzi. “Ndi munthu wabwinobwino kapena wopenga?” mnzungu uja anafunsa mnzake wakuda uja. “Muchezetseniko pang’ono mnzanu, eh? Mukhozanso kupanga kasewero, mukhoza kuchita chisudzo. Ineyo ndikhala woonerera, awirinu mukhala akatswiri a zisudzo.” “Nkhani ya zisudzoyitu ine ndiye si kwenikweni,” munthu waku- da uja anatero. “Ndipo ngati nditachita, ndingakonde kupanga mbali yomvetsa chisoni. Koma kuti ndikusangalatse, ndiyesetsa . . . Dzina lako ndi ndani?” anamufunsa Matigari. “Matigari ma Njiruungi.” “Matigari ma Njiruungi?” “Inde, mwabooleza.” “Ndiye ukufuna chiyani kuno?” “Ndikufuna makiyi a nyumba yanga.” “Ukudziwa kuti nyumbayi ndi ya ndani?” “Inde ndikudziwa! Ndi yanga. Nyumba imeneyi ndi ya ineyo komanso banja langa.” “Bob, akutitu nyumbayi ndi yake komanso ya banja lake . . . Zathe- ka bwanji kuti nyumbayi ikhale yako?” iye ankayankhula ndi Matigari modzipopa kwambiri ngati mmene amachitira wapolisi akamafunsa mafunso munthu woledzera. Funso lakuti, “Zatheka bwanji kuti nyumbayi ikhale yako?” linadzutsa mbozi ya khalee m’mutu mwa Matigari, ndipo ana- kumbukira zomwe zinachitika m’mbuyomo. Anapuma mousa moyo. Kenako anasiya geti lija n’kutembenukira munthu waku- da uja. Ndiyeno anayamba kuyankhula naye. Tsopano zinkango- khala ngati Matigari akufotokoza zinthu zozama kwambiri kwa mwana wamng’ono, m’chinenero chimene ndi ana okha 73