Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 72

Matigari Gawo 12 Mzungu komanso munthu wakuda anali atakwera pamsana pamahatchi aja ndipo anali ataima m’mbali mwa msewu waphula womwe unkalowa kugeti lina. Mahatchi omwe anakwerawo ankaoneka mofanana. Onse ankaoneka ofiirirako. Nayenso mzungu komanso munthu wakudayo anali atavala zovala zofanana. Chimene chinkawasiyanitsa unali mtundu wakhungu lawo basi. Koma tikakamba za mmene anakhalira pa- mahatchiwo komanso mmene ananyamulira zikwapu ndiponso zingwe zoyendetsera mahatchiwo, panalibe kusiyana. Komanso mmene ankatafunira chingerezi, panalibe kusiyana kulikonse. Zinkaoneka kuti anali akufuna kuti azisiyana. “Bwanawe, tionana kuphwando madzulo ano.” Ndiyeno ali mkati motsanzikana, anaona Matigari akuyenda molunjika pamene anaimapo. Kenako anaimitsa mahatchi awo n’kudikirira kuti aone kuti munthuyo akufuna chiyani. Guthera ndi Muriuki anali ataima penapake kuseri kwa zi- yangoyango zina ndipo ankangodikira kuti aone zomwe zitachi- tike. Onse ankadzifunsa kuti: ‘Koma mutu wa munthu ameneyu umakoka, kapena mawaya ena anaduka? Si nyumba zimenezi zinali za atsamunda omwe anali m’dziko muno ndipo panopa ndi za anthu ena olemera kwambiri, monga anthu ochokera m’mayiko ena komanso ena a konkuno a mitundu yosiyana- siyana—akuda, makaladi komanso azungu? Komatu Matigari ankachita zinthu mosatekeseka komanso mosakayika mpang’ono pomwe. Ndipo zimene ankachita zinkaoneka kuti akudziwa chimene akuchita. Iye anayenda n’kudutsa anthu anali pamahatchi aja ndipo anakafika pageti. 71