Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 68
Matigari
muno amene sakudziwa kuti apolisi akungokhalira kulimbana
ndi ana asukulu komanso ogwira ntchito?”
“Inde, ndi zimenetu apolisi masiku ano akumachita,”
anatero Muriuki. “Kodi si dzulodzuloli limene ogwira ntchito
ena anatidzimulidwa koopsa, ena anafika mpaka pothyoledwa
dzipalapasiro.”
“Tiyeni tikoke phazi kuti tikawapeze azimayiwo
asanaweruke.” Anatero Guthera.
Kenako anaima paphiri pafupi ndi chikanga china. Kutsogo-
lo kwawo kunali minda ya tiyi, yomwe kumalekezero kwake
sikunkaoneka. Inkangokhala ngati yopanda malire. Tiyiyo anka-
duliridwa bwino zedi moti ukamamuonera patali, ankangokhala
ngati kapinga.
“Nthakayi ndi yachonde zedi.” Anatero Guthera.
“Kodi malo onsewa ndi a munthu m’modzi?”
“Inde, ngati si a munthu ndiye kuti ndi a kampani yakunja.”
Ndiye popeza sankaona munthu aliyense wogwira ntchito
m’mindayo, anaganiza zotsetsereka kudutsa m’tinjira tamkati
mwa tiyiyo kuti awafufuze. Anayenda kwa nthawi yaitali koma
sanakumane ndi aliyense mpaka anakafika kumunsi
kwenikweni. Mundawo unali waukulu osati pang’ono.
Muriuki anatopa n’kuyenda moti ankamva kuphwanya
paliponse. Ndiyeno atayang’ana Matigari, anayamba kudabwa
kuti: ‘Kodi munthu ameneyu ndi wamtundu wanji? Sindina-
muone akudya chilichonse, koma sakuoneka kuti watopa nga-
khale pang’ono.’
Koma atayenda mtunda wautali osafikabe kumapeto kwa
mundawo, Guthera ananena kuti kuli bwino apeze malo oti
agone usikuwo, ndiyeno adzapitirize kusakako tsiku lotsatira.
67