Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 66

Matigari “Komatu mindayi ndiye ilipo yochuluka zedi, ndiye ndinga- kayambire kuti?” Matigari anatero akukhala ngati akudziyank- hulira yekha. Guthera anaganizira funsolo kwa kanthawi. Kwa nthawi yonse yomwe ankayankhulanayo, Guthera ankasakasaka mpata woti ayamikirire zimene Matigari anamuchitira zija. Umenewu unali mwayi wake ndipo anali ataupeza tsopano. Iye ankafuni- tsitsa kusonyeza chiyamikiro chake kwa Matigari kaya mutu wake umagwira kapena ayi. Mumtima anadziuza kuti: “Ndipita nawo limodzi. Ndikawathandiza mpaka atapeza banja lawo.” “Tiyeni ndikuperekezeni kumunda wina wapafupi.” Guthe- ra anauza Matigari. “Ndiponso zingakhale zophwekerako kuti ndizikafunsa ineyo chifukwa kumakhala azimayi okhaokha.” “Tiyeni tinyamuke,” Matigari anatero akuimirira. “Tiyeni ti- nyamuke mdima usanagwe.” Matigari anali asanadye chakudya chake chija. Mayi m’modzi wogulitsa mubalayo anamumangira chakudyacho papepala. Matigari anatenga chakudyacho limodzi ndi botolo la mowa lija n’kuzilongedza m’thumba la chijasi chake. 65