Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 62

Matigari umakuotcha ndi mkute wadzulo! Mvula ikakuona litsiro sikata. Anthuwo atangomuona, onse analikumba liwiro. Ankati: “Mwana wachigawenga ujatu ndi ameneyu! Tikachita masewera tikhoza kuputa naye mavuto.” Nthawi zonse ankati akapita kutchalitchi ankabwerako chimanjamanja.” “Tsiku lina, mtsikanayo anaganiza zoyamba kuyendayenda m’tauni. Tsiku limenelo anabwera ndi kawokomani ka ufa. Ndikufuna kukutsimikizirani kuti: Kungoyambira tsiku li- menelo, anayamba kupeza zakudya komanso zovala za abale ake aja. Koma sankapeza ndalama zokwanira kuti akanawa- tumiza kusukulu kapena malo ena omwe akanapita kukapalira tsogolo lawo pophunzira maluso osiyanasiyana.” Si pano ndi awo ndimakumana nawo m'mabala komanso m'mashopu aku- dya zotoleza m'mabini komanso akupempha azungu kuti awathandize m'misewumu? Nkhani yanga yathera pamenepa. Koma mwina sindinayankhebe funso lanu. Kungochokera tsiku limene mtsikanayo anayamba uhule, analumbira kuti: ‘Ngakhale kuti mavuto ndi amene achititsa kuti ndisiye kuyenda m'njira yachiyero n’kukhala hule, sindidzayerekeza kuyenda ndi wap- olisi. Ndizichita uhule ndi anthu ena omwe sindikuwadziwa monga akuba komanso zigawenga. Koma sindidzayerekeza kuyenda ndi anthu oipa mitima amenewa, ngakhale atandilonje- za kuti andipatsa thumba lamakobidi.’ Anasankha kuti awonje- zere lamulo limeneli pamwamba pa malamulo khumi aja. “Pali Akhristu a mitundu iwiri,” anatero Matigari ndipo zimene ananenazo zinadulako bata lomwe linali pamalopo pam- buyo poti Guthera wamaliza kunena mbiri yake ija. “Ena ama- konda dziko lawo, pomwe ena amaligulitsa. Palinso mitundu iwiri ya asilikali. Ena amateteza anthu, koma ena amawazunza komanso kuwapha.” 61