Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 61

Matigari zida. Munthu amene wapezeka ndi zipolopolo popanda laisensi amayenera kunyongedwa. Koma ineyo ndikufuna ndikuthan- dize. Palibenso munthu wina kunja kwa polisi ino amene akud- ziwa za nkhaniyi. Ukangovomera kuti ugona ndi ine, timasula bambo akowa. Koma mtsikanayo anamenyetsa nkhwangwa pamwala. Iye anayankha kuti: ‘Sindingachite zinthu zomwe zin- gakhumudwitse atate wanga wakumwamba. Iye anapereka lamulo lakuti: Usachite chigololo.’ Koma wapolisiyo anamuuza kuti: ‘Basitu, bambo ako wawapereka kuti akaphedwe, moti sudzawaonanso.’ Kenako bambo ake aja anaphedwadi. Malo awo analandidwa ndi boma ndipo mtsikanayo anatsala ndi chiudindo chosamalira abale ake aja. Kenako mavuto anayamba kuunjikana. Umphawi, usiwa komanso chakudya chinkasowa. Analibiretu chilichonse. Ana ena aja anayamba kulira kuti: ‘Kodi bambo ali kuti? Kodi lero tidya chiyani?’ Mtsikanayo ankangowayang’ana akusowa chonena. Iye ankati akaganizira kuti akanatha kupulumutsa bambo ake, ankadziimba mlandu kwambiri. Ankati akamva abale ake aja akulira ndi njala, mtima wake unkamupweteka zedi. Ankadziuza kuti: ‘Kodi tsopano ndizingoonerera abale angawa akufa ndi njala? Ndaphetsa kale bambo anga, kodi ndilolera kuti ndiphetsenso abale angawa? Nkhani imeneyi inkamuzunguza mutu kwambiri. Koma atate wake wakumwamba sankayankha mafunso akewa. Zimene Bai- bulo linkanena zinali zoti: Usabe. Usasirire . . . kanthu kalikonse ka mnzako. Usachite chigololo. Koma kunena za njala, yankho panalibe. Nanga bwanji za ludzu? Yankho panalibenso. Nanga bwanji usiwa? Ayi ndithu. Ndipo kunyumba ana ankangokha- lira kulira: ‘Njala ikuwawa! Kodi bambo abwera liti? Kodi anapi- ta kuti?’” “Mtsikanayo anapitanso kwa wansembe uja. Iye anapempha anthu a m’tchalitchicho kuti amuthandize. Koma tsoka likalimba 60