Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 60

Matigari ‘Inde ndi zoona. Palibe chikondi chachikulu ngati ichi: kuti amuna ndi akazi apereke moyo wawo m’malo mwa anthu am- biri popita kumapiri komanso nkhalango. Limeneli ndi lamulo lalikulu kwambiri m’chilamulo cha Khristu, komanso ngakhale kwa Muhammad ngakhalenso Buddha.’ Mtsikanayo anazizidwa thupi atamva zimenezi moti kwa kanthawi anangokhala khuma. M'masiku amenewo kupezeka ndi zipolopolo unali mlandu wo- ti munthu ankanyongedwa nawo. Kenako mkulu wa apolisi uja anabweranso n’kutenga bambo ake aja n'kukawatsekera. Posa- khalitsa anatulukiranso, akumwetulira mwaudyabolosi. Iye anati: ‘Akuboma sindinawauze za nkhaniyi. Nkhaniyi tikhoza kuithetsa ngati iwe ndi ine titagwirizana. Ngati utavomera kuti ugona ndi ine, bambo akowa tiwatulutsa.’ Mtsikanayo sa- nayankhe kanthu. Mkulu wa apolisiyo anapitiriza kuti: ‘Ukudziwa kuti moyo wa bambo akowa uli m'manja mwako?” “Mtsikanayo anabwerera kunyumba ndipo atafika anazika maondo pansi n’kupemphera kwa atate wake wakumwamba n’kumupempha kuti amupatse nzeru komanso kumutsogolera. Tsiku lotsatira anapita kwa wansembe. Wansembeyo anatsegula Baibulo n’kumuwerengera Malamulo Khumi. Iye anati: Usakha- le nayo milungu ina koma Ine ndekha. Usaphe. Usachite chigololo. Uzilemekeza atate wako ndi amako . . . Kenako anati, ‘Pamenepa ndi pamene pagona chiyeso. Lamulo lina likuti, Usaphe. Lina likuti, Usachite chigololo; pomwe lina likuti, Uz- ilemekeza atate wako ndi amako . . .” Kenako onse anagwada pansi n’kupemphera. Wansembeyo anapemphera kwa Mulungu kuti apereke nzeru kwa mtumiki wake, kuti apitirizebe kuyenda m’njira yachiyero. Tsiku lotsatira, mtsikanayo anapitanso kupolisi kuja. Mkulu wa apolisi uja anabwerezanso kumuuza kuti: ‘Bambo akowa ali m’gulu la anthu omenyera ufulu wadzi- ko lawo. Ndipo agwidwa akuthandiza zigawenga pozipatsa 59