Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 59

Matigari “Choncho, iye anabadwanso mwatsopano. Anayamba kuta- manda Mulungu modzikhuthula, moti nthawi zina ak- amapemphera ankadzimva ngati wamera mapiko n'kuulukira kumwamba. Koma kenako nkhondo inayambika. Nkhondoyo inachititsa kuti anthu ayambe kugawikana. Ena anakhala ome- nyera ufulu wawo, pomwe ena anayamba kulimbana ndi ome- nyera ufuluwo. Dzikoli linangotembenukiratu. Ana anayamba kuukira makolo awo, makolonso anayamba kulimbana ndi ana awo. Atsikana komanso anyamata apachibale analumbira kuti apha abale awo. Koma mtsikanayo anatsimikiza mtima kuti azimvera anthu awiri okha pamoyo wake: Atate ake akumwam- ba komanso apadziko lapansi. Iye ananenetsa kuti adzachita chilichonse chotheka kuti azichita zokondweretsa atate ake awir- iwa. Bambo ake ankapita kutchalitchi sabata ndi sabata. Koma nawonso anali womenyera ufulu wadziko lawo. Mtsikana uja sankadziwa zimenezi. Nthawi zosawerengeka bambo akewo ankamuuza kuti: ‘Malamulo khumi onsewa ndi abwino, koma onsewa agona palamulo limodzi: Chik o nd i. Ndipo palibe chikondi choposa ichi: kuti munthu apereke moyo wake kuwombola anthu ambiri. Tangoganiza, anthu onse atakhala okonzeka kupereka moyo wawo m'malo mwa anthu ena, ko- manso m’malo mwa dziko lawo.’ Tsiku lina bambo ake apadziko lapansi aja anamangidwa. Apolisi anamuuza mtsikana uja kuti: ‘Bambo ako anapezeka atanyamula zipolopolo m’Baibulo.’ Mtsi- kanayo anakana kuti bambo ake akuwadziwa bwinobwino, ndi munthu wabwino moti sangachite zimenezo. Koma mkulu wa apolisiwo anamuuza kuti, ‘Dikira tiwabweretse kuti uwafunse wekha.’ Kenako anabwera nawo unyolo uli m’manja. Mtsi- kanayo ataona bambo akewo, anagwetsa misozi. Kenako wap- olisi uja anachokapo kaye. Iye anawafunsa bambo ake aja kuti, ‘Zimene akunenazi ndi zoona?’ Bambo akewo anayankha kuti, 58