Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 58

Matigari anthu awiri pamoyo wake: Atate ake wakumwamba omwe ana- mupatsa moyo komanso atate ake apadziko lapansi omwe ankamulera mwachikondi kwambiri. Atate ake apadziko lapansi ankakonda ana awo zedi. Iwo sankadya chakudya pokhapokha aonetsetse kuti ana onse akhuta. Iwo sanka- kondera mwana aliyense. Kwa iwo ana onse anali ana ochokera kwa Mulungu, zolengedwa zake, ndipo onse anali ofanana. Ngakhale anali osiyana ngati zala za m’manja, onse ankafunika kusamaliridwa mofanana. Mtsikanayo sankalephera kupita kutchalitchi ndiponso kupemphera kwa Mulungu wake. Ali kutchalitchiko, anaphunzira Malamulo Khumi. Koma atakula anayamba kuwerenga yekha malamulowo. Iye anaphunzitsid- wa kuti azisunga malamulo amenewa nthawi zonse, kulikonse kumene ali, kaya ena akumuona kapena ayi.” Usakhale nayo milungu ina koma Ine ndekha. Usadzipangire iwe wekha fano losema. Usatchule dzina la Yehova Mulungu wako pachabe. Uzikumbukira tsiku a Sabata, likhale lopatulika. Uzilemekeza atate wako ndi amako . . . Usaphe. Usachite chigololo. Usabe. Usamnamizire mnzako . Usasirire . . . kanthu kalikonse ka mnzako. “Cholinga chake chachikulu chinali choti asamachite zoipa. Iye ankafuna kumachitira ena zinthu zabwino. Ankafuna kutsatira njira ya chilungamo komanso kukhala ndi khalidwe loyera.” 57