Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 57

Matigari wina kuti amwe.” Onse anakhala n'kumamwa zakumwa zawo ndipo palibe ankayankhula. Ngakhale azimayi aja ankayankhula motsitsa mawu kwambiri ngati akuopa kuti wina awatapa m’kamwa. “Chinachitika n'chiyani kuti apolisiwa azilimbana nawe chonchi?” Matigari anafunsa Guthera. Guthera anakhala ngati akukayikira kuti ayankhe kwinaku akuyang'ana Muriuki. Zinkakhala ngati sakufuna kufotokoza Muriuki ali pomwepo. Koma kenako anaganiza zotambasura nkhani yonse. “Nkhani imeneyi sindinayambepo ndauza munthu,” anayamba motero. “Mungachite bwino kudzifunsa kuti n’chifu- kwa chiyani ndimapezeka kubala kuno? Dikirani ndkuyalireni zonse zomwe ndakumana nazo pamoyo wanga.” “Kalekalelo, kunali mtsikana wina wodzisunga. Mayi ake anamwalira pamene mtsikanayu ankabadwa. Mtsikanayu limodzi ndi azichemwali komanso azichimwene ake, an- aleledwa ndi bambo awo achikondi. Bambowo anali Mkhristu wokonda kupemphera ndipo anali mkulu wampingo. Mtsi- kanayo nayenso anakula akuopa Mulungu. Iye ankapita ku Church of Scotland pomwe bambo ake ankapita ku Independent Church. Chochititsa chidwi n’choti bambo akewo sankamuletsa kupemphera tchalitchi china. Iwo ankati chofunika kwambiri ndi kutsatira Mawu a Mulungu komanso malamulo ake ndipo ankaona kuti chipembedzo sichidzapulumutsa munthu, koma mtima. Iwo ankati chipembedzo cholondola chili mumtima. Mawu omwe sankachoka pakamwa pawo anali akuti matchalitchi angokhala nyumba zomwe anthu amakumanamo kuti alambire Mulungu. Mtsikanayo ankakonda kwambiri 56