Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 49

Matigari anatero ndipo pamene ankayankhula anatembenuka n’kuona Matigari ndi Muriuki. “Bolanso kupempha mowa kwa munthu amene sindikumudzidwa, ngati bambo akhala apowo.” Guthera anachoka panali anzake paja n’kupita kumene kunali Matigari ndipo mosachedwachedwa anamukhalira pamiyendo n’kukoloweka mikono yake m’khosi mwa Matigari akumuyang’ana ndi diso lachikondi. “N’chifukwa chiyani mukundiyang’ana choncho dadi? Mukuonekansotu kuti mwaiwala kudya chakudya komanso kumwa mowa wanu. Ine ndimamwa mowa wangati juwisi womwewu. Sindikonda zitsulo. Uum! Musanyade, monga simundigulira umodzi? Ngatinso mukufuna zina ndi zina ndikhoza kukutchipitsirani. Muli ndi zingati? Anthu enatu ama- dulitsa, mukudziwa? Koma popeza pano ndi pakati pa mwezi, iliyonse yomwe munthu ali nayo timalandira. Ndipo nthawi zi- na timatha kulola ngongole. Mukhoza kudzandipatsa mwezi ukatha. Koma ndimalola zimenezi pokhapokha ngati munthu ali pantchito. Muli pantchito eti? Kapena mumachita ulimi wang’ombe zamkaka? Kapena muli ndi munda wakhofi? Mukhozanso kukawaponda akazi anu ndalama zomwe agulitsa tomato kunsika lero. Musadandaule, ife bola munthu atipatse chilembwe basi, sitilabada kaya zachokera kuti. Koma nthawi zi- na timakumana ndi mavuto. Mwachitsanzo, ngati ogwira ntchi- to atachita sitiraka, sindikudziwa kuti ndipeza kuti ndalama zo- gulira chakudya. Masiku sakoma onse, lero umati kuseka, mawa kulira. Komabe sitimataya mtima chifukwa nthawi zina azimu amatha kutigwera m’mbale. Timatha kukumana ndi azibambo omwe agulitsa malo. Kodi nanunso muli ndi malo? Mukhoza kugulitsa ngakhale a mkazi wanu, mukhozanso kugulitsa nga- khale nyumba yake. Mukagulitsa eti da?” 48