Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 48

Matigari Gawo 9 “Bwanji? Waba chiyani?” “Ayi, sindinabe kanthu. Kungoti wapolisi wina amandifuna. Akumangokhalira kunditsata ngati ntchentche. Kaya akuganiza kuti ndikumufuna. Akanakhala wanzeru akanachita manyazi. Eti kumandiimbira likhweru n’kumandiuza kuti ndiime. Ndani wamisalayo yemwe angaime n’kumacheza ndi wapolisi dzuwa likuswa mtengo! Ndiyetu akam’fune wosewera naye. Munthu wake si ine ayi!” Matigari atamuona Guthera, anaona kuti mtsikanayo ndi njole yeniyeni, chiphadzuwa. Mano ake anali oyera ngati mkaka, tsitsi lake linali lambiri, lakuda bwino komanso lofewa. Zinkangokhala ngati nthawi zonse amalipaka mafuta a mtsatsi. Iye sanali wamtali komanso sanali wamfupi. Sanali wonenepa komanso sanali woonda. Zimene anavala zinkamukhala ngati analengedwera momwemo. Khosi la Matigari linakhala ngati latha girisi chifukwa linkakanika kutembenuka n’kuchotsa maso kuchoka kumene kunali mtsikanayo. Mumtima mwake ankati, “Tangoonani kansalu kokongola kali yaliyali paphewako.” Kansaluko kanali katagwera pachifuwa. Sinali nkhani ya- masewera kuchotsa diso lake pa mtsikanayu. Analidi mtsikana woika pachiyeso ngakhale m’busa yemwe analumbira kuti sadzapenyetsetsa namwali. Ndani ananena kuti nawonso abusa alibe maso. Maso alije mpanda. Komabe Matigari ankadzifunsa kuti, “Kodi mtsikana wokongolayu akudzataniko kubala kuno?” Kenako azimayi aja anagundika nako kuseka. “Apolisiwo atani Guthera? Sumawakonda? Ndalamatu ndi ndalama, sitimalabadwa kuti zachoka kuti.” “Ineyo ayi. Ndalama za apolisi zimanunkha magazi,” iye 47