Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 46
Matigari
Matigari anapita kukakhalanso patebulo paja ndipo
anamupeza Muriuki atatanganidwa kwambiri ndi kugalika
zakudya zake. Atakhala pansi, ankangoyang’ana chakudya
chake chija ngati sakuchifuna, moti sanachikhudze ngakhale
pang’ono. Iye ankangodzifunsa mafunso ambirimbiri.
Ankaganizira za Muriuki komanso anthu ake onse. Pamene
ankatuluka munkhalango muja, ankaganiza kuti
kusonkhanitsanso anthu a m’banja lake kukhala kophweka.
Koma tsopano zinkaoneka kuti ntchito ilipo. Dzuwa linali
litayamba kupendeka, ndipo anali asanakumane wachibale
wake ngakhale m’modzi. Sankadziwanso kuti ayambira pati
kuwasakasaka.
Kenako azimayi aja anatsegula wailesi.
. . . Mwatsegulayi ndi Wailesi Yanu ya Choonadi. Tsopano
timvetsera pulogalamu ya azimayi. Lero tikambirana nkhani zokhudza
banja . . . Msonkhano wapachaka wa Chitukuko cha Amayi
unatseguliridwa ndi mkazi wa Nduna Yoona Zachilungamo dzulo.
Mkazi wa ndunayo anauza azimayi kuti kuchita chigololo komanso
kumwa mowa n’kumene kukuchititsa kuti mabanja ambiri apasuke
m’dziko muno. Mayiwo analimbikitsa akazi onse kuti azilimbikira
kupemphera komanso kuti asiye kupikisana ndi amuna awo pa nkhani
ya kumwa mowa komanso kuchita chiwerewere. Iwo anati mzimayi
ndi munthu wofunika kwambiri pakhomo ndipo ndi amene
angachititse kuti banja lake liziyenda bwino.
Kenako Matigari anati: “Zoonadi mayi ndi wofunikadi
pakhomo. N’chifukwa chiyani sindinaganize zimenezi
poyamba paja? Ndikanayamba ndi kufunafuna mayi kaya!
Ndiyeno ndikapeza mayi, andiuza kumene kuli ana. Mayi ndi
amene amasunga mtundu komanso kusamalira malo.”
45