Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 45

Matigari moto uja unakolera nyumba yonse moti mayi anga anapsera momwemo.” Matigari anaingitsa ntchentche yomwe inkauluka pafupi ndi khutu lake. Ntchentcheyo inkangokhala ngati yatumidwa. Itaona kuti ikhoza kuonetsedwa zakuda, inathawa n’kuzungulira kangapo kenako inakatera pafupi ndi zenera. Matigari ataona kuti yatera, anatembenuka n’kuyang’ana Muriuki. Mumtima mwake ankangoti: “Kodi idzafika nthawi pamene ana amasiye adzapukute misozi yawo n’kuyamba kuimba lokoma?” Mayi uja anawabweretsera chakudya komanso zakumwa zomwe anaitanitsa. Zitangoikidwa patebulo, Muriuki anayamba kutsopa botolo lake la zakumwa zoziziritsa kukhosi. “Botolo langalo musalitsegule,” anatero Matigari. Kenako anaimirira n’kupita kukasukusula pampope wina womwe unali pafupi ndi chimbudzi. Magazi omwe anali pankhope yake anayamba kusungunuka ndipo ankachititsa kuti madzi amene ankakhera pansi azioneka ofiira. Atamaliza kusukusulako, anapha ludzu lake pomwa ndi dzanja lake madziwo mofanana ndi mmene imachitira ngamila yaludzu. Mayi anawabweretsera zakudya uja anabwerera komwe kunali mnzake uja ndipo anakakhala pansi. Azimayiwa anapitiriza kukambirana nkhani ya sitiraka ija. Mabotolo awiri a theka anali patsogolo pawo. M’modzi wa aziyiwo ankaluka mosonyeza kuti anazolowerana nazo kwambiri moti zinkaoneka kuti ankachita zimenezo asakuganiza n’komwe. Ndiyeno mayi ankalukayo anauza anzake onse kuti: “Tiyeni timvetsere pulogalamu ya azimayi ija. Nthawi yake yangokwana kumene.” Kenako anadzuka n’kupita kukachotsa nyimbo inkalira ija. 44