Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 41

Matigari sidikira ngakhale mfumu!” “Kodi unamvapo zokhudza anthu a m’banja langa kufakitaleko?” “Anthu a m’banja la Matigari?” anafunsa Ngaruro. “Kodi inuyo mukuganiza kuti ifeyo tili m’banja la ndani?” ananena mawu amenewa kwinaku akumweturira. “Ukawauze anthu a m’banja langa kuti: ‘Mtsamunda Williams tamutsogoza. Nayenso wantchito wake John Boy tamutsira dothi m’nkhutu. Tsopano tiyeni tibwerere kunyumba, tikayatse moto komanso tikamange nyumba yathu limodzi.’” “Taimani kaye,” Ngaruro anatero, akuoneka kuti wazindikira zinazake. “Williams? Boy? Mmodzi mwa mabwana athu pafakitaleyi amadziwika ndi dzina loti Williams. Robert Williams. Wachiwiri wake dzina lake ndi John Boy.” “Osaiwalatu kuti dzina ndi moto,” Anatero Matigari. “Zoona,” Ngaruro anayankha. “Uthenga mwandiuzawu ndikafikitsa. Tikakakumana ndikawauza kuti: ‘Mtsamunda Williams tamutsogoza. Nayenso wantchito wake John Boy tamutsira dothi m’nkhutu.’ Ndikasonkhanitsa anthu onse a m’banja mwanga n’kuwauza kuti: ‘Tsopano tiyeni tibwerere kunyumba, tikayatse moto komanso tikamange nyumba yathu limodzi.’ Anzeru akazindikira zimene ndikutanthauza.” Ngaruro wa Kiriro anauyamba ndipo zinkangokhala ngati Matigari wamupatsa mangolomera. Matigari ndi Muriuki anamuperekeza ndi maso ndipo anaonanso namtindi wa ogwira ntchito ukulowera kufakitale kuja. Kenako Ngaruro analowa m’chigulu cha ogwira ntchitowo ndipo sanaonekenso. Nthawi ya nkhomaliro inali itangotsala pang’ono kutha. Ndipo anthu ambiri tsopano 40