Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 40

Matigari Pamalowo panali bala yadenga la malata yomangidwa ndi miyala, ndipo chakumapeto kwa balayi kunali malo ogulitsira zakudya. Malowa anali omangidwa ndi matabwa ndipo denga lake linali lofoleredwa ndi mapepala. Panalinso kampanda komangidwa ndi makatoni ndiponso masaka. Anthu ankatha kugula chakudya chawo n’kudyera malowa kapena kukadyera mubala ija. Koma ambiri ankasankha kukhala pomwepo ndipo munthu unkatha kuwaona atatanganidwa ndi kujegweda chakudya chawo. Pepala la mitengo ya zakudya zomwe zinkagulitsidwa pamalowa linamatidwa pakhoma. MATAHA HOTELO, BARA NDI RESITILANTI Ugali wa Nyama Yowotcha ndi Supu; Nsima ya Masamba ndi Nyemba; Nsima ndi Chipere; Tchana; Soya; Tiyi; Mkaka; Phala; Chapate, Buledi, Samusa, Masikono ndi Zina TIMAGULITSA CHILICHONSE KUPATULAPO CHIMENE SIMUDYA Ogwira ntchito kufakitale kuja anali atayamba kubwerera tsopano. Anthuwa ankabwerera m’magulu a anthu atatu, anayi komanso asanu. “Ineyo ndisalowe koma,” anatero Ngaruro. “Tinagwirizana kuti tipite mofulumira lero chifukwa kukakhala msonkhano wa ogwira ntchito onse panja pafakitale. Tikufuna tichite sitiraka.” “Mukufuna mupange sitiraka?” anafunsa Matigari. “Inde, tiyamba kunyanyala ntchito 2 koloko masanawa . . . Umumu mupeza chakudya chilichonse chomwe mungakonde kudya. Mupemphe madzi kuti mupukute magazi ali kunkhope kwanuwo. Ineyo ndithamange. Nthawi sikudikira ine, ndipo 39