Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 39
Matigari
kenako ndinatulukira m’minda yanthochi. Ndinawoloka
mitsinje, ndinakwera mapiri mpaka ndinakalowa m’nkhalango.
Mtsamunda Williams ananditsatira ndipo panayambika
nkhondo ya wafawafa kuti zioneke kuti wamphamvu anali
ndani komanso kuti bwana m’chipetachi anali uti.”
“Mmenemutu ndi mmene zinayambira kuti tilimbane kwa
zaka zonsezi.”
“Ndi dzulodzuloli pamene zaoneka kuti wamphamvu ndi
ndani. Mtsamunda Williams wabwira dothi! Ndamuonetsa
kiyama! Nditam’kantha, ndinamuzemberera n’kufika pamene
anagwera kuti ndikatsimikizere kuti wafadi. Analidi atasiya
gaga. Ndinamuponda pachifuwa n’kutenga mfuti yake
n’kuilozetsa m’mwamba ndipo ndinayamba kuimba nyimbo
yachipambano posangalala kuti ndagwetsa mdani wanga.”
“Ndiye lero ndi limene ndatuluka m’nkhalango n’kubwera
kuno. Ndikufuna ndisonkhanitsenso banja langa.”
Pamene ankafotokoza zimenezi, maso ake ankawala ngati
nthanda. Zimene ankanenazi zinamufika pamtima Muriuki
komanso Ngaruro wa Kiriro moti sanazindikire zoti afika
pamalo ogulitsira zakudya paja. Nkhaniyi inali itawaponyera
patali, kale kwambiri pamene mauta ndi mivi ya adani
inkagwedeza mitengo ndi mitsitsi yomwe, mwinanso ngakhale
kutekesa mapiri.
“Ndiye ndi angati amene atsala m’nkhalango kuti moto wa
ufulu wathu usazime?” Ngaruro wa Kiriro anafunsa motero.
“Limenelo sindiyakha, funsa lina?”
“Chabwino, basi ndamvetsa. Tafika tsopano. Malo ogulitsira
zakudya aja ndi amenewa.”
38