Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 38

Matigari nyumba yake. Tuluka m’nyumba mwangamu msanga. Iwenso manja uli nawo ako! Munthu wankhanza komanso wadyera ngati iwe sindinamuonepo! Pita ukamange nyumba yako. Ukapanda kutuluka m’nyumba yangayi uona mbonaona. Ndi ndani anakunamiza kuti womanga alibe maso kuti awone, mutu kuti aganize komanso lilime kuti ayankhule?’” “Pamene ndinkamaliza kunena zimenezi n’kuti ndikunjenjemera ngati mtengo mumphepo yankhuntho. Sindinkanjenjemera chifukwa chozizidwa kapena chifukwa cha mantha. Ndinkanjenjemera ndi nkwiyo. Ndinali ndi nkwiyo womwe unabwera mamba a umbuli wa zaka zambiri atathothoka m’maso mwanga. Tsopano ndinali nditayamba kuganiza ngati munthu.” “Nthawi yomweyo Mtsamunda Williams anagwira thenifolo. Nane ndinathamangira pomwe ankasunga mfuti yake ndipo ndinaitengadi. Ndinaitenga n’kuigwira m’manja. Kenako ndinagwada ndi bondo limodzi nditamulozetsa mfutiyo. Koma ndikukuuzani padzikoli sipadzaleka kuchitika zodabwitsa! Simungakhulupirire zimene zinachitika. Ndi John Boy, munthu wakuda ngati ine ndemwe, wantchito wa Mtsamunda Williams, yemwe anamupulumutsa. Sindikumbukira bwinobwino kuti anatulukira kuchokera kuti. Mwina ankachokera kukhitchini. John Boy anandilumphira kumsana kwinaku akukuwa. Mfuti ija inagwera pansi ndipo tinayamba kulimbana pamene paja. Ndinkafunitsitsa nditatenganso mfutiyo. Koma Mtsamunda Williams anabwera kudzamuthandiza John Boy. Ndiye ndinaona kuti popanda mfuti , zinthu zindidera. Choncho ndinakokera mphamvu, n’kutsomphoka m’manja mwa John Boy. Kenako ndinalumpha n’kutulukira pazenera. Ndinathawira m’minda ya tiyi, n’kulowa m’minda ya chimanga, 37