Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 37

Matigari Koma ndikamati ndiyambe kusangalala kuti ndapambana, ndinkamva zoti anthu ena amuona ali penapake, akundifunafuna kuti andiphe. Nthawi zina zipolopolo zake zinkandilowa m’nthupi. Ndinkakwawa, kuyenda motsimphina n’kukabisala kuphanga mpaka bala langa litapola. Nthawi zinanso ankangotsala pang’ono kundizimitsa. Mwamwayi Mulungu ankakhala asanakonzeke kundilandira mu Ufumu wake. Koma kodi mukudziwa kuti tinkalimbirana chiyani?” “Nyumba. Nyumba yanga.” “Mwaona, ndinamanga nyumba ndi manja anga. Koma Mtsamunda Williams anayamba kugonamo ine n’kumagona pakhonde. Ndinkalima minda yomwe inazungulira nyumba yangayo, koma ndi Mtsamunda Williams amene ankakolola mbewu zake. Iye ankangondisiya kuti ndizikunkha zotsala za m’mundamo. Ndinkagwira ntchito yotopetsa m’mafakitale, koma Mtsamunda Williams ankatolera ndalama zonse n’kumakazivundika kubanki ndipo ineyo ankandiponyera kakhobidi kuti ndikagulire m’gaiwa. Ndalama zonse zomwe tinkapanga zinkatafunidwa ndi mtsamunda ameneyu. Ndikuganiza kuti mukudziwa bwino mbiri imeneyi. Ndinkalima mbewu ndi manja angawa, koma zokolola zonse zinkatengedwa ndi Mtsamunda Williams. Dzikoli ndi lopanda chilungamo ntheradi! Dziko limene telala amavala nsanza, mlimi kumadya zotoleza, m’misiri womanga kumagona pakhonde. Ndiye nditatopa nazo, tsiku lina ndinaganiza zothana naye. Ndinamuuza kuti, ‘Mtsamunda Williams, umakolola pomwe sunafese, tsopano imva kulira kwa mphalasa komanso lipenga la chilungamo. Telala akufuna zovala zake. Mlimi akufuna nthaka yake komanso zotsatira za thukuta lake lomwe wakhala akukhetsa zaka zonsezi. Womanga akufuna 36