Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 36

Matigari “Anthu amenewa ndi amene analowa m’thengo kukamenyera ufulu wathu wodzilamulira.” Ngaruro anayankha motero. “Anthu amanena kuti ena mwa anthu amenewa adakali kunkhalango.” “Chifukwa chiyani?” “Akufuna kuti moto wa ufulu wathu usazime,” Ngaruro anayankha. “Chifukwa?” “Sizingakhale bwino motowo utazima. Kodi ukudziwa kuti moto wa ufulu wathu unayatsidwa m’nkhalango komanso m’mapirimu zaka zambiri zapitazo?” Ngaruro anapitiriza motero. “Zoonadi,” anatero Matigari. “Anawa sangadziwedi nkhani imeneyi, achepa nazo. Tangoganizani zimene zachitikira ineyo. Ineyo ndi Mtsamunda Williams takhala tikulimbana kwa zaka zambiri m’mapiri komanso m’nkhalango zimenezi. Tinkasakanasakana m’mapanga, m’mitsinje, zigwa komanso malo ena osiyanasiyana. Nthawi zina ndinkatha kumuona ali chapatali, koma pamene ndinkati ndimulase nacho chipolopolo, ndinkangozindikira wazimiririka m’tchire, kenako sankaonekanso chifukwa cha mdima wa m’nkhalango.” “Nthawi zina ankandipezeketsa. Koma akamafuna kuti andiwombere ndinkakhala ndathawa. Ndinkagudubuka pansi, kukwawa komanso kuyenda ngati njoka ndipo ankalephera kundigwiranso. Zimenezi zinachitika kwa masiku, miyezi, komanso zilumika zambirimbiri.” “Palibe amene ankafuna kugonjera mnzake. Nthawi zina ndinkamuombera n’kumaganiza kuti ndamutumiza ku Gehena. 35