Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 35

Matigari “Usadandaule,” bambo uja anatero kwinaku akudzuka mwamphamvu ngati wabwereranso ku unyamata. Anachita zimenezi modzilimbitsa mtima ngakhale ankamva kupweteka. Anatolanso zinthu zake zija, maso ake akuyang’ana ngati akuone zomwe zidzachitike m’tsogolo. “Tipitira limodzi kunyumba yanga. Ndikutengera kunyumba yanga kuti ukaone zoti sikuti ndinangotaya nthawi yanga pachabe pomenya nkhondo yolimbana ndi Mtsamunda Williams . . .” Ngaruro ndi Muriuki anayang’anizana modabwa atamva mawu amenewa. Iwo ankadzifunsa kuti, “Kodi makwinya onse anali pankhope pake aja alowera kuti?” “Dzina lanu ndi ndani?” Anafunsa motero Ngaruro wa Kiriro. “Matigari ma Njiruungi.” “Matigari ma Njiruungi?” “Inde, dzina langa ndi limenelo.” Anayenda molunji kumsika kuja ndipo aliyense sankayankhula mnzake. “Matigari ma Njiruungi,” Ngaruro anabwerezanso dzina lija. “Anthu omwe anapulumuka nkhondo yomenyera ufulu wathu.”* *Matigari ma Njiruungi (Gikuyu): Tanthauzo lenileni la mawuwa ndi, “anthu omwe anasemphana ndi zipolopolo”—Anthu omenyera ufulu wawo omwe anapulumuka pankhondo yolimbana ndi atsamunda komanso amene anapulumuka ku maulamuliro ena omwe anayamba kulamulira pambuyo pake. “Ukuwadziwa eti?” “Ayi, ndinangomva mbiri yawo.” “Kodi anthu omenyera ufulu ndi ndani?” Muriuki anafunsa. 34