Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 33

Matigari Madalaivala anaima aja nawonso anapitiriza ulendo wawo. Eni maokala anapitiriza kugulitsa malonda awo ndipo ogwira ntchito kufakitale anapitirizabe kuyenda kwinaku akukambirana nkhani zomwe zinkachitika pafakitaleyo. Iwo ankakambirana za kunyanyala ntchito komwe ankafuna kuyambe kuchitika masana a tsikulo. Analibe nazo ntchito zoti mdala anagendedwa koopsa uja anali kwala pansewu, ali chikomokere. Mwana anathawa uja, anatulukira atagwira dzanja munthu wina yemwe ankagwira ntchito pafakitaleyo ndipo ankasonyeza munthuyo bambo anali chigonere pansi uja. “N’chifukwa chiyani akutuluka magazi chonchi?” munthuyo anamufunsa mwanayo pamene ankatulutsa kansalu kopukutira mamina n’kuyamba kusunsa magazi pachipumi komanso pakhutu la bamboyo. Bamboyo anatsitsimuka ndipo atangotsegula maso, anaona mwana uja akuoneka wachisoni zedi. “Mwana wanga, zikomo kwambiri kuti sunandisiye ndekha?” bamboyo anatero. “Ayi,” mwanayo anakana akuyang’ana pamene magazi a bamboyo anayenderera. “Sindidzakuiwala mwana wanga,” bamboyo anatero. Kenako anazindikira kuti mwanayo anali limodzi ndi munthu wina yemwe ankamupukuta magazi pankhope yake. 32