Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 32

Matigari Bamboyo ankadzifunsa mafunso ambirimbiri koma sankapeza mayankho. Mafunso onsewo ankangoloza ku funso lalikulu limodzi lakuti, “Kodi ndi ndani watipepetula kuti tiyambe kumenyana tokhatokha? Ndi ndani amene wapereka temberero kuti ana ndi makolo awo azimenyana, mdani wawo akuwonerera mosangalala.” Chimene chinkamuteteza kuti mwala usamufike chija chinakhala ngati chamusiya tsono. Kenako mwala unamugagada pakhutu lakumanja. Ankangomva ngati khutulo lathothokapo. Ataligwira, dzanja lake lonse linanyowa ndi magazi. Mwala wina unafikira m’mutu ndipo unanyamula chipewa anavala chija n’kukachigwetsera kumbuyo kwake. Kenako anatembenuka n’kuwerama kuti achitole. Pamene ankaweramuka, mwala wina unamukang’antha pachipumi. Anamva ululu woopsa moti anataya pansi chipewa komanso chijasi chija. Iye ankatha kumva zitseko za magazi zikutseguka komanso ululu woopsa ukukolera ngati moto kumutu kwake. Mtsinje wamagazi unafwamphukadi kuchokera m’mphuno, m’kamwa komanso m’makutu mwake. Ana aja ankangokhala ngati agalu olusa omwe akukanganirana nyama moti anayamba kuvunga matalala a miyala kwa bambo uja. Ankangokhala ngati akupha galu wachiwewe. Miyala yonseyo inatera pa bambo uja moti nkhope yake inakupukakupuka. Kenako anagwera pansi ngati thumba la mbatata, n’kukomoka. Mtsinje wa gulu la ogwira ntchito kufakitale aja unafika pamene bamboyo anagwera ndipo gululo linakhala ngati lamumiza. Gulu la ogwira ntchitowo linkangoyenda ngati palibe chimene chimachitika. Ana aja anasiya kamodzim’kamodzi kugenda ndipo anabwerera kumudzi wawo. 31