Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 28

Matigari “Anafa akumenyera ufulu . . . ” bamboyo anatero, akuoneka kuti maganizo ake ali kutali. “Omenyera ufulu wa dziko lathu, mafakitale athu komanso nyumba zathu.” “Ali kuti?” mwanayo anafunsa akuoneka kuti akufunadi kudziwa yankho la funso lakeli. “Komadi, kaya ali kuti?” bamboyo anabwereza funsolo ngati kuti nayenso akusinkhasinkha yankho lake. Koma mwana uja anamudulira kutsogolo n’kumuuza kuti: “Basi, mukhoza kubwerera pano. Nyumba zathu zija ndi zimenezi.” Pa nthawiyi n’kuti atangodutsa nyumba zina zosanjikizana. Kutsogolo kwawo kunali manda a galimoto zosiyanasiyana. Ziphapha za galimoto monga Ford, Mercedes-Benz, Volkswagen, Peugeot, Volvo, Fiat, Datsun ndi zina, zinali nduu pamalowo. Analidi manda enieni a ziphapha za galimoto. Ena anali opindikapindika, ena ophwanyikiratu moti anangotsala zitsulo zokha, kungosiya mbiri yoti nthawi inayake inali galimoto. Malowa kunalidi kunsitu kwa galimoto zosiyanasiyana. Ziphapha zokutha kwambiri zinali zitaphimbidwa ndi makatoni, mapepala apulasitiki, masaka, nsalu komanso zinthu zolekanalekana. Zina zinali zitakhazikidwa pamiyala pomwe zina, mkati mwake munkamera udzu. “Zimenezi ndiye nyumba zathu!” anatero mwana uja. “Izizi?” “Inde, umenewu ndiye mudzi wathu. Aliyense wa ife ali ndi nyumba yake. Nyumba yanga ndi Mercedes-Benz,” mwanayo ananena zimenezi monyadira kwambiri mokhala ngati akuuza bamboyo kuti nyumba yakeyo ndi yapamwamba kuposa za ena 27