Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 272

Matigari *Sisi mbwa kali. (Kiswahili): Kutanthauza " Ndife agalu olusa." Mwadzidzidzi, kunaoneka zing'aning'ani, ndipo ziphaliwali zingapo zinawomba. Kenako madontho angapo amphulupulu anayamba kuthonya. Posakhalitsa chimvula chinayamba kupwatamuka koopsa. Gulu la asilikali komanso apolisi lija linafika m'mbali mwa mtsinje muja. Ena anali adakali pamsana pamahatchi ndipo ena anangoimaima. Ankaoneka kuti anali ndi njala yaikulu yogwira munthu. Koma chifukwa cha zimene zinachitikazi mkwiyo unawayakira chifukwa anati atataya ndalama yokwana mapaundi 5,000, omwe anali atangogwera kumene mumtsinjewo. Apa n’kuti mtsinjewo ukukukuma ndi madzi omwe anadzadza chifukwa cha chimvula chija. Iwo anayenda m'mbali mwa mtsinjewo akuganiza kuti aona matupi a Matigari ndi Guthera akuyandama pamwamba pa madzi kapena atatsakamira penapake. Ankadzifunsa kuti, ‘Kodi afadi kapena athawa? Kodi Matigari ndi ndani kwenikweni?’ Mvulayo inakhuthuka koopsa ngati kuti zitseko zakumwamba zatseguka ndipo madontho ake ankangokhala ngati akuchokera mundowa. Kungochokera nthawi imeneyo, mphekesera zinkamveka kuti mvula imene inagwayo ndi imene inazimitsa moto wonse womwe unayatsidwa ndi magulu a anthu olusa aja. M'madera onse a m'dzikoli, ana anatuluka panja n'kuyamba kuimba kuti: Mvula, mvula bwera lero, kuti ndikuphere mwana wang'ombe. Ndi winanso wokhala ndi mabelu m’khosimu! 271