Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 271

Matigari Matigari ankatha kumva phokoso la madzi a mumtsinje uja bwinobwino tsopano. Masitepe angapo ankanalumphira mumtsinjemo . . . ndipo akanawolokera tsidya lina . . . Koma atangotsala pang'ono penipeni kuti alumphe, agalu ena anamuwakha. Ena onse anabwera n'kuwaunjirira. Agaluwo anakhadzula Matigari ndi Guthera mwankhanza kwambiri. Anang'amba zovala zawo komanso minofu yawo ndi mano awo okhala ngati misomali. Koma ngakhale nthawi imodzi, Matigari sanasiye Guthera ngakhale pang'ono. Magazi awo anali chuchuchu ndipo ena analowa munthaka pafupi ndi mtsinje uja. Apolisi komanso asilikali anali pamahatchi aja anathamangira kunali agalu kuja. Ngakhalenso aja ankayenda wapansi analiyatsa liwiro, kunjonjola kuti akakhale oyamba kugwira munthu ankafunidwa kwambiriyo. Matigari anasonkhanitsa mphamvu zake zonse ndipo atagwirabe Guthera m'manja mwake, anayamba kukwawa ndi mawondo ake kulowera kunali mtsinje kuja. Pamene ankakwawapo n'kuti agalu ena omwe anali atagagada mwamphamvu miyendo komanso matako ake akukhwekhwerekera pansi. Agaluwo ankakhala ngati apana nyama yoti adye, moti ankalolera kukhwekhwerezedwa pansi koma sanamusiye. Kenako Matigari ndi Guthera anagwera mumtsinje. Madzi anathovokera m'mwamba ndipo ena anagwera m'mbali mwa mtsinjewo momwe munali mouma gwa. Kenako agalu aja anaima m'mbali mwamtsinje muja, malilime ali lawilawi ngati alandidwa nyama. Ena ankasetekera magazi omwe anali pamphuno zawo. Ndipo ena ankalira mwaukali kwambiri ngati akuuza dziko lonse kuti: Sisi m bwa kali.* 270