Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 261

Matigari zimenezi moti analepheratu kuletsa khamulo, lomwe linkayen- da ngati madzi osefukira. “Nyumba ya Boy ikuyaka! Nyumba ya Boy ikuyaka!” ankaimba choncho. Anthu ena ankafuna kulowa m’nyumbayo kudzera pawin- do lomwe silinkatuluka utsi. Iwo ankafuna alowe m’nyum- bamo n’kukaba katundu. Aliyense ankafuna kuti atengemo ke- nakake, ngakhale kochepa bwanji. “Nyumba ya munthu woipa Boy ikuyaka! Nyumba ya munthu woipa Boy ikuyaka!” chuni cha nyimbo ija chinayamba kusintha. Utsi woopsa womwe unayamba kutuluka m’nyumba ija unabweza anthu omwe ankafuna kulowera pawindo aja. Malilime a moto walawilawi ankathamuka kuchokera mkati mwa nyumbayo n’kumagwera panja. Khamu la anthu aja lina- yamba kubwerera m’mbuyo, ndipo anaima mozungulira nyumbayo mofanana ndi mmene anthu amachitira ak- amapereka mpata kwa anthu omwe akukutumulana. Iwo anapitirizabe kuimba: Motoo, moto wayakaa, moto wayakaa, moto wayakaa. Tiyeni tiwothe motoo, moto wayakaa, moto wayakaa. Motoo, moto wayakaa, moto wayakaa, moto wayakaa. Tiyeni tiwothe motoo, moto wayakaa, moto wayakaa. Iwo anaima mozungulira nyumbayo akuimba mwam- phamvu nyimboyi ndipo ena ankakuwa kuti, “Nyumba ya Boy ikuyakaa . . . ” Wapolisi ankatsogolera anzake uja anaitanitsa wapolisi wina yemwe ankayankhula ndi wailesi meseji uja. Mkulu wa apolisiyo anaitanitsanso apolisi ena chifukwa zinkaoneka kuti khamu la anthulo likhoza kuwapweteka. Iwo ankaopa kuti 260