Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 256

Matigari Magalimoto a apolisi aja anapitirizabe kumulondola. Matig- ari ankatha kuwaona pagalasi loonera zinthu zakumbuyo. Ko- ma anazindikira kuti ngakhale kuti galimoto za apolisiwo zi- nali zaliwiro kwambiri, apolisiwo sankayerekeza ku- muyandikira kwambiri. Iye anamvetsa chifukwa chake. Iwo ankaganiza kuti ali ndi mfuti. Iye anadziuza kuti, ‘Si paja pawailesi analengeza kuti anthu omwe aba galimotoyo ali ndi zida zoopsa?’ Matigari anafuna kuseka. Koma pamene kusekako kunkati kuziyambika, mkwiyo unamubwerera ata- dziwa kuti apolisi atseka njira zonse zomwe akanadutsa kuti akafike kumene anakwirira zida zake kuja. Matigari anatsimikiza mumtima mwake kuti zivute zitani, salola kuti Boy amubere tsogolo lake lonse. Koma ankadzifunsa kuti, ‘Kodi ndikafika bwanji kumtengo wakachere uja?’ Koma kenako anatsimikiza mumtima mwake zinthu zimene ankafuna kuchita. Nyumbayo inali yake. Ankadziuza kuti an- zeru ndi amene amapambana. Anaona kuti angotengera chitsanzo cha zimene a Iregi anachita poukira boma. Kenako anatenga msewu wolowera kumene kunali nyumba kuja. Apolisi aja anapitirizabe kumulondola, atayatsa magetsi apadenga la galimoto zawo ndipo nyalizo zinkangokhala ngati zikuzungulira mumdima womwe unali madzulowo. Masailini anali pokopoko kumveka mwaphokoso kwambiri. Iye anadabwa kwambiri pamene anatulukira munsewu womwe unkalowera komwe kunali nyumbayo. Zinkangokhala ngati anthu a m'dziko lonselo asonkhana kunyumbako. Gal- imoto zinali zitaimikidwa mbali zonse. Panalibiretu malo omwe munthu akanaimika galimoto yake m'mbali mwa nsewuwo. Kumalowa kunali fumbi. Nawonso asilikali anali yakaliyakali paliponse atanyamula mifuti ndi matochi. Magetsi a panja 255