Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 255

Matigari pakati kuti asowe kothawira. Apolisiwo ankaganiza kuti aka- muopseza achita mantha n'kulowetsa mateyala ake m'ngalande zomwe zinali m'mbali mwa nsewuwo kapena kungoima. Ke- nako mosamala kwambiri, Matigari anaponda buleki, ndipo ankawonjezera moto pang’ono kuti galimtoyo isangoima ka- modzinkamodzi. Galimoto za apolisi zija nazonso zinabweza moto chifukwa ankaganiza kuti Matigari akuima. Komatu apa Matigari ankangodzikonzekeretsa! Iye anayamba watsimikizira kaye kuti panalibenso galimoto ina kuwonjezera pa awiriwa, imene inkabwera. Ataona kuti ndi ziwiri zomwezo, anatembenuka mwadzidzi- dzi ndipo anayamba kuyendetsa galimoto molowera kumene ankachokera kuja. Apolisiwo anadzidzimutsidwa kwambiri, ndipo posakhalitsa anangozindikira adyana okhaokha. Pamene ankafufuza kuti chikuchitika n'chiyani, Matigari anali atatha mtunda. Kenako magalimoto awiri aja anayamba kumuthamangitsa. Iye ankadzifunsa kuti, ‘Kodi akapolo amenewa adziwa bwanji kuti ndine ndikuyendetsa galimoti imeneyi? Kodi mwina kazitape uja ndi amene wawauza?’ Kenako anakumbukira kuti mkazi wa nduna uja anakanena kupolisi kuti galimoto yake yabedwa. Mzimayiyu anachita mwayi chifukwa munthu ankachita naye zopusayo anali dalaivala wake osati munthu wina wapadera. Akanakhala munthu wina, akanaganiza kawiri asanakanene kupolisi kuti galimoto yake yabedwa. Komabe mwina akananena kuti munthu amene anali nayeyo anangokwera nawo galimotoyo basi. Matigari anadziuza kuti, ‘Kodi nanenaso ndikuganiza chiyani? Kuganizira zimenezi sikungandithandize mpang’ono pomwe. Ukaziputa limba. Mwana wang’ona sakulira dziwe limodzi! 254