Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Página 254
Matigari
wamwamuna. Galimoto ya apolisi inkangomulondola. Zinali
zoonekeratu kuti inkathamangitsa iyeyo. Ataona izi, Matigari
anaponda latalata ndipo kunali kuthamangitsana.
Matigari sankadziwa choti achite. Iye ankafuna ataimitsa
galimotoyo kenako n'kuyamba kuthawa wapansi kupita kunk-
halango kuja. Koma ankaona kuti akhoza kugwidwa. Iye
anayamba kukayikira komanso kudziimba mlandu. Ankaona
kuti akanachita bwino akanayamba wapita kunyumba kuja. Ko-
ma ankadziuza kuti, ‘Ndiye ndikanatenga bwanji chinthu chom-
we ndinachikhetsera thukuta m'manja mwanga mulibe chida?’
Galimoto ya apolisi ija inayamba kuyandikira. Matigari
anapitirizabe kuponda moto, iye ankafuna kuchita zinthu zoti
awasokoneze apolisiwo. Zikanakhala kuti panali msewu wina
wam'mbali, akanatenga umenewo. Koma ankadzifunsa kuti,
‘Nanga bwanji nsewuwo utakhala kuti watha kutsogoloko?’ Ko-
mabe sanataye mtima. Iye anapitirizabe kuyang’ana m'mbali
mwa nsewuwo kuti mwina aona penapake poti angakhote.
Ankaganiza kuti mwina apeza penapake poti akhoza
kutembenuka, mwina pamene msewu ukukhota kapena palan-
dabauti.
Mwadzidzidzi, anangozindikira kuti galimoto ina yatulukira
kutsogolo kwake. Galimoto imeneyinso inali ya apolisi. Apatu
anali pampanipani, pakati pamagalimoto a apolisi awiri omwe
ankamuthamangitsa. Koma kodi akanathawa bwanji?
Magetsi a pamwamba pa galimoto ya apolisi anayamba ku-
wala. Nawonso apolisi aja anayamba kumuunika ndi matochi
awo, n'kumamupatsa chizindikiro choti aime. Galimoto inali
kutsogolo kwake ija inkayenda mbali yofanana ndi imene
Matigari ankayenda ija, ndipo kumbuyo kwake kunali ina
yomwe inkamutsatira ija. Iwo ankafuna kuti akumane naye
253