Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 253

Matigari Munthu aliyense ali ndi manja ake, ayenera kumawag- wiritsa ntchito m'malo mongowalongedza m'thumba n’ku- mayembekezera kuti ena amugwirire ntchito.” Mawuwa anakhala ngati apanga nyimbo m'maganizo mwake. Iye ankaimba nyimboyi mobwerezabwereza. Pamene ankaimba nyimboyi, anakumbukira zimene anakambirana ndi Ngaruro wa Kiriro. Ngaruro anamuuza kuti m'dzikomo munali magulu awiri a anthu. Panali gulu la anthu olamulira mopondereza anzawo komanso mamesen- jala awo, oyang'anira, apolisi ndi asilikali. Chipani cholamu- la ndi chimene chinali mamesenjala amenewa ndipo ndi amene ankalamulira boma, malamulo komanso asilikali. Mfundo komanso chikhalidwe ndiponso mbiri yadziko, yomwe inkalembedwa inali m'manja mawo chifukwa iwowo ndi amene ankanyamula uthenga . . . Kumbali inayi, kunali gulu la anthu ogwira ntchito, ali ndi zimene amakhulupirira, chikhalidwe chawo komanso mbiri yawo. Mamesenjala achipani cholamula aja ankayesetsa kutseka pakamwa mbiri ya ogwira ntchitowa pomanga anthu ake n’kumaka- watsekera kundende kuti zoona zenizeni zisadziwike. ‘Kodi zimenezi zichitika mpaka liti,’ anadandaula Ngaruro, ‘Kodi anthu apirira ulamuiro wa mamesenjala komanso mabwana awowa mpaka liti? ‘Mpofunika chilungamo chioneke! Chioneke kwa anthu amene akuponderezedwa,’ Matigari anadziuza choncho. In- de chilungamo chimapita kwa oponderezedwa ngati atachita zinthu mogwirizana kwinaku atatenga zida n'kumalimbana ndi adani awowo . . . Kenako anayang'ana pagalasi loonetsa zinthu zam'mbuyo. Anazindikira kuti m'mbuyo mwake mukubwera mbola. Kenako anaponda moto mwana 252