Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 252

Matigari Gawo 19 Matigari analowa mumsewu waukulu. Pa nthawiyi n'kuti kunja kutayamba kuvala m’dima. Iye anaponda latalata, ndipo mwendo wake unaponda m’mafuta moti galimotoyo inaulukira m’tsogolo. Matigari ankaganizaganiza kuti apite kunyumba kuja komwe anthu anasonkhana kuti akawaone zimene zikuchitika. Koma kamtima kena kankamuletsa kuti akatenge kaye zida zake. Iye sanalole kuti chiyeso choti akaone athuwo chimu- gonjetse. Ankaona kuti chilungamo chimabwera kwa oponde- rezedwa ngati anthuwo atachita zinthu mogwirizana n'kuyamba kulimbana ndi adani awowo ndi zida. Iye anali atamasula kale lamba wamtendere. Ankafuna abwerere kunkhalango kuja n'kukavala lamba wake wazipolopolo kuti akalimbane ndi adani ake. Ankaona kuti akapanda kuchita zimenezi ndiye kuti anthu ake asowa kolowera, asoweratu mtengo wogwira. Ankadziwa kuti si nzeru kuti apitirizebe kukhetsa thukuta lake n'kumapin- dulitsa nthata zosayamika zomwe zimangokolola pamene sizinalime. Iye ankayembekezera kudzaona tsiku limene mavuto onse adzathe. Kungoti sankadziwa kuti zidzachitika liti. Ankayembekezera kuti nthawi idzafika pamene: Omanga azidzakhala m'nyumba zapamwamba, Atelala azidzapha ulusi, Alimi azidzadya zakudya zonona. ‘Ayi, si chilungamo kuti anthu apitirize kukhetsa thukuta kuti apindulitse nthata zomwe zimakolola pomwe sizinafese.’ Mumtima mwake anatero. Ife matelala sitikufuna kuti tisanduke mapoto omwe amaphi- ka koma osadya nawo. 251