Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 250

Matigari “Anthu akukhulupirira kuti munthu wina wotchedwa Matigari ma Njiruungi yemwe wathawa kuchipatala cha anthu amisala m'mawa wa lero, akufuna kupita kunyumba kwa Boy kuti akailande mwachiwawa. Apolisi akufuna akamugwire an- thu onse akuona. Ngati mutandifunsa ineyo kuti ndikuuzeni maganizo anga, ndikhoza kukuuzani kuti munthuyo si wopenga.” “N’chifukwa chiyani mukutero? Munthu wake ndi wotani?” “Anthu ena akumanena izi, ena akumanena izi. Ena akumanena kuti ndi wamtali komanso wooneka ngati chiphona ndipo ena akumati ndi wamtali moti akhoza kugwira kumwam- ba. Ena akumanena kuti ndi wamfupi ngati chitsa, pomwe ena akumanena kuti ndi mwana. Palibe amene akudziwa kuti mun- thu ameneyu ndi wamtundu wanji. Zikumvekanso kuti amatha kuyankhula zinenero zosiyanasiyiana. Ndinamva ena akunena kuti munthu wake amakonda kuyenda yekha. Pomwe ena akumanena kuti nthawi zonse akumayenda ndi mwana ko- manso akumatsatiridwa ndi mzimayi. Akumati ukhoza ku- muona, koma kenako kungozindikira wasowa. Akumatsala ndi mzimayi ndi mwana uja basi. Zikumamveka kuti ali uku, ena akumati takumana naye uku. Akumapezeka paliponse. Ziku- mavuta kuti ndiye munthu ugwire chiti. Zikanakhala kuti sin- digwira ntchito ku kampani yogulitsa mafuta yakunjayi, bwenzi nanenso ndili komweko.” Matigari analipira ndalama ya mafuta aja ndipo anayamba kuyenda molowera kumene kunali Mercedes-Benz kuja. Asanatsegule chitseko chagalimotoyo, anaima kaye n'kuponya- ponya maso. Iye anaona munthu anamuona akusuta fodya uja akutuluka muofesi ija. 249