Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 247
Matigari
Gawo 17
Zinali zoona kuti aliyense ankayembekezera kuona
chozizwitsa tsiku limenelo. Asilikali komanso apolisi anali
ponseponse. Iwo ankafuna kugwira Matigari wamoyo kapena
wakufa. Ankafunitsitsa kuchita zimenezi anthu akuona. Anka-
ona kuti zimenezi zipheratu mphekesera zonse zonena za
zozizwitsa, angelo komanso kubweranso kwachiwiri kwa
Khristu zomwe anthu ankazinena mosinjirira. “Ofunika tiwa-
sonyeze anthuwa bwinobwino, awone ndi maso awo tiku-
musenda chikopa Matigari amamutamayo,” mkulu wa apolisi
analangiza apolisi anzake.
Kunyumba kwa Robert Williams komwe John Boy anapita
kukabisala kunali apolisi ambirimbiri olondera. Boy anakhala
pafupi kwambiri ndi lamya n'cholinga choti akhale woyambirira
kumva za kumangidwa kapena kuphedwa kwa Matigari. Ndipo
mofanana ndi anthu ena onse, Williams komanso Boy,
ankadikirira kuona chozizwitsa. Koma ankachita zimenezi
kumtima kuli bi! John Boy ankatuluka thukuta m’kamwa.
Atolankhani anyuzipepala zosiyanasiyana maso anali kun-
jira, kudikirira kubwera kwa Matigari.
Atolankhani a wailesi yakanema ankatutira zipangizo zawo
kumalowa. Ndipo onse maso anali kunjira.
Munthu aliyense yemwe anali kumalowa ankadikirira chin-
thu chimodzi: Ankadikirira kuona chozizwitsa chikuchitika. Ko-
ma pa nthawi yomweyo, onse ankadabwa. Ankadzifunsa kuti:
Kodi Matigari ma Njiruungi ndi ndani kwenikweni? Kodi ndi
munthu womenyera ufulu wadziko? Kodi ndi mngelo Gabrieli?
Kodi ndi Yesu Khristu? Kodi ndi munthu wamnofu ndi magazi,
kapena ndi mzimu? Kodi ndi mneneri woona kapena wabodza?
246