Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 240
Matigari
"Yesu adzakupezani muli m'tulotu . . . akamadzabwera."
"Ngati mulibe nkhani yoti mundiuze ingokhalani, mu-
sayambe kundilalikira za Yesu ine ayi."
"Kodi mumamudziwa mkazi wanduna ija? Nduna Yoona
Zachilungamo ija? Iye limodzi ndi womuyendetsa anaukiridwa
ndi zigawenga moti zawabera galimoto."
"Zoona?"
"Ndamva zoti amapita kumpikisano wamahatchi . . . kuti
akaone mmene hatchi yomwe anagula mogwirizana ndi Aga
Khan ikathamangire . . . "
"Kodi nawonso anthu akuda ayamba kumagula mahatchi a
mpikisano?"
"Maendeleo ya muafirika, maedeleo ya wanawake . . . *" Komanso
pali zina. Zikumveka kuti akubawo ananyamula zida osati
masewera. Anamangirira zida ndi m’mano momwe!
*Maendeleo ya muafirika, maedeleo ya wanawake (Kiswahili): Kutanthauza kuti " Amuna a
mu africa akamatukuka, azimayinso amatukuka."
Matigari ankafuna kuseka moti anavutika kwambiri kuti
adziletse. Kenako anawoloka nsewu.
"Ingodikirani mdima ugwe. Ndikatenga AK47 yanga pomwe
ndinaikwirira," Matigari anadziuza mumtima, "Ndipo
ndikabwerako palibe atandifunenso!"
239