Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 237

Matigari "Amangokhaliranso kukamba zamtsogoleri wadziko lino." Muriuki anawonjezera. "Ingodikirani muone!" Koma kwa kan- thawi, wailesi ija sinanene zamtsogoleri wadzikolo, Pulezidenti Ole. Guthera anayamba kumuseka Muriuki. . . . Zigawenga zoukira boma ku El Salvador zaphulitsa mlatho womwe uli kulikulu la dzikoli ndi bomba. Zigawengazi zanena kuti sizisiya kuchita zamtopolazi mpaka boma la USA komanso antchito awo achikuda a ku El Salvador atavomereza kuti m'dzikomo muchitike chisankho . . . Tsopano mvetserani nkhani zakwathu konkuno: Mtsogo- leri wathu wa dziko lino, Pulezidenti Ole . . . "Ndinakuuzatu ine! Ndinanena ine!" Muriuki anakuwa mot- ero akusangalala ngati waponda mu ufa, ulosi umene ananena utakwaniritsidwa. Guthera ndi Muriuki anayamba kuseka koopsa. Koma sanaseke kwa nthawi yaitali. . . . Monga mmene munamvera posachedwapa, wamisala m'modzi, Ngaruro wa Kiriro wamwalira kuchipatala china atawomberedwa . . . Ngaruro anawomberedwa ndi apolisi ataopseza kuti ayambitsa zachi- wawa— "Ayi inuu!" Guthera anatero mwachisoni. Aliyense anangokhala chete. Kenako anadutsa mafamu a khofi, tiyi, gonje komanso zi- nanazi. Ndiyeno anadutsa timinda tina toguga tomwe tinkachi- ta kuoneka kuti tatoperatu ndi kugwira ntchito. Pamenepa mpamene Matigari anayankhula. "Padzikolidi pali magulu awiri a anthu omwe ndi osiyana kwambiri," ananena zimenezi mokhala ngati akubwereza mawu a Guthera aja. "Pali anthu omwe amamenyera ufulu wadziko lawo komanso ena omwe amaugulitsa motchipa." 236