Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 233

Matigari Nyumba ankazidutsazo zinali zazikulu molapitsa, komanso zinali ndi mabwalo aakulu a maluwa. Panja pake panali kapinga komanso mitengo yobiriwira bwino. M'malo olowera m'nyumbazi munali mageti akuluakulu azitsulo. Munthu aka- madutsa munsewu ankatha kuona madamu osambirira odzadza ndi madzi abuluu. Ngakhale kuti m'dzikomu munali chilala, nyumbazi zinali ndi madzi okwanira kuthirira kapinga komanso maluwa. Zinalinso ndi madzi okwanira kudzadzitsa madamu akuluakuluwo. Pageti iliyonse panali mlonda ndipo pambali pake panali galu wamkulu. M’mipandayi munalinso zikwang- wani zolembedwa kuti: "Mbwa Kali." *Mbwa Kali (Kiswahili): Kutanthauza " Chenjerani. Kuli agalu olusa." "Kumene tabwera kuno kukungokhala ngati dziko linatu! Ngati si kwathu komwekunotu." Guthera anatero, ndipo zimene ananenazi anangokhala ngati waimba ng'oma yowambawamba chifukwa ndi zimenenso Muriuki ankafunanso kunena. Msewu umene ankayendawo unalibe mabampu. Nthawi ndi nthawi ankafika pamalo ochitira chipikisheni ndipo aka- mayandikira, apolisi ankangowabayibitsa kwinaku akutsegula chotchingira nsewuwo kuti Mercedes-Benz'yo idutse bwinob- wino popanda kuchepetsa liwiro. Muriuki ankalakalaka atatsegula windo n'kuyang'ana apolisiwo. Iye ankafuna atawauza kuti, "Ndifeyotu amene mukuwafunafuna aja!" kapena kuwauza kuti, "Uyu ndi Matigari ma Njiruungi." Iye ankalakalaka ataona zimene apolisiwo akanachita atazindikira zimenezi. "Galimotoyi ikungokhala ngati tikiti yolowera kumwamba ndithu!" Muriuki anatero mosangalala. 232