Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 224
Matigari
Kenako anaona Muriuki akuyandikira Mercedes-Benz ija. Iye
anayenda mozungulira galimotoyo n'kuipitirira pang'ono.
"Zikutheka bwanji kuti woyendetsa galimoto asatuluke kuti
ataye madzi?" Guthera anafunsa.
"Ndi ndani amene anakuuza kuti oyendetsa magalimoto
akaima amafunika kutaya madzi?"
"N'chifukwa chiyani mwayamba poyerayera kuwaikira kum-
buyo oyendetsa galimoto? Kodi nanunso munali woyendetsa
galimoto?"
"Ndani, ineyo? Palibe ntchito yomwe ungaitchule yomwe
sindinagwirepo. Ndachita chilichonse chimene ungachiganizire
ndipo zonsezi ndinkachitira atsamuda osayamika aja."
Kenako anaona Muriuki akubwerera. Atamuona anayamba
kumudikira ndipo Muriuki anabwerako akumwetulira mwau-
tambwali.
"Ndi ndani?" Guthera anafunsa.
"Ndi mzimayi ndi mzibambo," Muriuki anatero, akuyesetsa
kudzigwira kuti asaseke.
"Akuchita chiyani?"
Muriuki anayamba kuseka koopsa. Guthera anayang'ana
Matigari, yemwe sanasinthe mmene ankaonekera.
"Anzanu ali m'chikondi. Achotsa zovala zonse. Ayatsa
wailesi, koma akuoneka kuti sakumvetsera wailesiyo."
"Asiyeni amenewo. Tiyeni tizipita." Anatero Matigari.
"Tiwasiye chifukwa chiyani?" Guthera anafunsa.
"Ndamva pawailesi akulengeza kuti apolisi atseka misewu
yonse ikuluikulu. Komanso alengeza kuti aliyense amene ataone
223