Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 223

Matigari Anali wokondwa zedi. "Minyangayotu amagulitsa ndalama zankhaninkhani. Kodi si paja munanena kuti pali atambwali ena omwe amagulitsa chimanga chadziko lino kumayiko ena? Amakhala akusinthanitsa chimangacho ndi makobidi ankha- ninkhani moti amalemera koopsa. Ndi zimenensotu zimachi- tika ndi minyanga ya njovu. Amaigulitsa kwa anthu ena adyera ochokera m'mayiko a amwenye komanso ku Ulaya. Amawononga zinthu zachilengedwe n’cholinga choti apeze chilembwe." "Kodi akapoli amenewa sadziwa kuti zinyama ndi mabwen- zi a anthu? Pamene tinali kunkhalango sitinkapha nyama mwachisawawa pokhapokha ngati tili ndi njala kapena ngati chakudya chatithera. Ndipo nthawi zina tikaona nyama yovulala, tinkaisamalira poimanga pamene yavulalapo. Nyama zinali zofunika kwambiri kwa ife. Zinkatichenjeza kukamabwera zoopsa. Kodi umadziwa kuti anthu amatha kuyankhula ndi zinyama? Ngati utadzakhala munkhalango kwa nthawi yaitali nawenso udzaphunzira kuyankhula ndi zinyama. Nthawi zina nyama imatha kukuyankhula. Umafu- nika kungokhala chete, n'kuimvetsera. Kodi ukuganiza kuti abusa aziweto amakwanitsa bwanji kukhala zakazaka m'tchire muno chinachake osawavulaza? Iwo amakhala anapanga mgwirizano wapadera ndi zinyama ndipo zinyamazo zim- awachenjeza kukamabwera zoopsa." "Anthu omwe amayendetsa magalimoto opuma ngati ame- newa amakhala kuti akolopola ndalama za ogwira ntchito om- we akungothimbirira ndi umphawi. Amangowalima anzawo pamsana basi," anatero Guthera. 222