Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 221

Matigari wanenayotu ndi yolondola." "Pali kusiyana kwakukulu pakati pa anthu ndi zinyama," Guthera anawonjezera mosonyeza kuti akuganizira zinazake. "Anthu akhoza kusunga chakudya munkhokwe ndipo ngati atachita zimenezi chakudya chikayamba kusowa sangama- khaule ndi njala. Zimenezitu zikutanthauza kuti anthu aka- mavutika ndi njala amakhala kuti achita kufuna." Matigari anayang'ananso Guthera mokhala ngati sanayambe wamuonapo. "Zimene ukunenazitu ndi zoona zenizeni." anabwerezanso Matigari. "Vuto ndi lakuti zinthu zonse zimene anthu ambiri amapeza zimalowa m'matumba a nthata zoyamwa anzawo magazi. Ama- gulitsa chakudya chonse n'cholinga choti maakaunti awo aku- banki asefukire ndi ndalama. Ndithudi abale, ndodo ya chitsiru ndi imene munthu wochenjera amathyolera mango chitsirucho chikusakasaka miyala yogendera mangowo," anatero Guthera. "Panopa ndi pamene ndamvetsa chimene mwakhala muku- chimenyera nkhondo kwa zaka zonsezi. Simukufuna kukhala ngati chitsiru. Simukufuna kumawedza nsomba n’kuika mum- tanga kuti nthata zoyamwa ena magazi zizibwera n’kukuwedze- rani mumtangamo!" Anthu anali m'galimoto aja sanatsikebe. Kenako Matigari anaitana Muriuki: "Achimwene, basi tsikani mumtengomo." Muriuki anatsikadi n'kupita pamene panali Matigari ndi Guthera. "Ndikufuna ndikutume. Uyende molowera kumene kuli gal- imotoyo ndipo uziyerekezera kuti ndiwe m'busa wang'ombe 220