Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 220
Matigari
Gawo 14
"Ndiye kuti nsewu tinaoloka uja suli kutali?" Guthera ana-
funsa.
"Muriuki, takwera mumtengowu uone kuti ndi ndani,"
Matigari anatero.
Muriuki anakwera mumtengo muja. Kunalibe nsewu pafupi.
Koma zinali zoonadi kuti ankaona galimoto. Galimotoyo
inkayenda ngati nkhono. Kenako inaima pafupi ndi ziyango-
yango zina chapataliko pang'ono ndi pamene anaimapo.
"Ndi Mercedes-Benz! Mercedes-Benz!" Muriuki anakuwa.
"Koma tsopano yaima."
Matigari ndi Guthera anachoka pachigompholera chimene
anabisala. Kenako anayamba kuyang'ana kumene kunali galimo-
to kuja. Inalidi galimoto yakuda yamtundu wa Mercedes-Benz.
Kenako anayamba kudikirira kuti amene anali m'galimotomo
atuluke.
Chapatali pang'ono kuchokera kumene kunali galimotoyo
kunali gulu la nkhosa komanso ng'ombe. Kupatulapo zinthu
zimenezi, m'chigwacho munalibenso chilichonse ndipo ukayan-
g'ana mbali zonse, chigwacho chinkakhala ngati chilibe malire.
"Kodi ziweto zimenezi zikudya chiyani padzuwa ngati
pamenepa?" Guthera anafunsa, akuloza kumene kunali nkhosa
ndi ng'ombe kuja.
"Mkaka umachokera kung'ombe, ndipo ng'ombe zimadya
nsipu. Choncho ngati nyama zilibe chakudya ndiye kuti anthun-
so asowa mkaka woti amwe. Choncho ngati ndafunsa za
ng'ombe, ndiye kuti ndikunenanso za abusa oweta ng'ombezo."
Matigari anayang'ana Guthera n'kunena kuti, "Mfundo
219