Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 218

Matigari Koma kungoyambira dzulo pamene ndinaphwanya lamulo langa la khumi ndi chimodzi, ndinayamba kusankha ndekha zo- chita. Ndikanatha kusankha kuchita zimenezo kapena ayi. Ko- ma ndinachita kufuna ndekha kuti zimene ndimafuna zitheke." "Koma sikuti zimenezi ndi zimene ndikufuna ndikuuzeni. Ndakhala ndikudziwa kuti moyo umene ndimakhala m'mbuy- omu unali ngati wachinyama. Moyo wanga sunali wosiyana mpang'ono pomwe ndi wanyama yakutchire yomwe imapuma, kudya, kumwa kenako n'kupita kukagona kwinaku ikudikirira tsiku lakufa. Chimene ndikunenera zimenezi si kokha chifukwa choti ndazindikira kuti ndakhala ndikukhala moyo wopanda cholinga chenicheni m'mbuyomu. Ndikudziwa kuti palibe mzi- mayi amene sadziwa mavuto osaneneka amene azimayife tima- kumana nawo." "Chomwe chikundisowetsa mtendere ndi ichi: Munthu akadziwa zoyenera kuchita, kodi amangokhala n'kupinda manja ake? Kodi kungodziwa zinazake ndi kokwanira? Kodi ndi zo- kwanira kuti ndingonena kuti tsopano ndazindikira? Ndikufuna kuchita chilichonse chomwe ndingathe kuti ndichotse zinthu zimene zikuchititsa kuti anthu azikhala moyo ngati zinyama, makamaka azimayi. Kodi palibe chilichonse chimene azimayife tingachite kuti tisinthe zinthu pamoyo wathu? Kapena tingopi- tiriza kutsatira njira imene amuna atipangira, kuti basi amuna azingowongolera moyo wathu? Kodi mesa m'dziko muno ambi- ri ndi azimayi? Tiyeni tizipita! Kuyambira lero ndikufuna ndikhale mayi woyambirira kumenyera ufulu wathu. Sindilola kuti ndizingokhala kumbuyo nthawi zonse. Matigari, yendetsani miyendo yanu kuti zipolopolo zilire ngindee! 217