Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 213

Matigari Gawo 13 Matigari, Guthera ndi Muriuki anali atakhala pansi pa mtengo wina kuyesa kuti apezeko kanthunzi ngakhale kuti mtengowo unalibe masamba. Dzuwa linkawamba, kunja kunka- tentha kuposa muuvuni ndipo linawawaula osati pang'ono. Udzu unali utafoteratu chifukwa cha kutentha. "Dzuwalitu ndiye likuchititsa kuti kutenthe ngati moto, mwati sitiyamba kufuka kaya! Tikayerekezera ndi dzulo lija ler- olo tikungokhala ngati tili m'chiwaya chomwe chili pamoto." anatero Guthera. "Indedi, dzulo lija nyengo yake simadziwika bwinobwino," anayankha motero Muriuki. "Sitinganene kuti kunja kumatentha kapena kumazizira." "Kutentha kumenekutu kukhoza kukudwalitsa, dzuwa ku- wala ngati enaake alituma." anawonjezera motero Guthera. Matigari anali atagona. Iye anagwiritsa ntchito chijasi chake chija ngati pilo. Nkhope yake anali ataivindikira ndi chisoti chake chija. Pa nthawiyi anaganiza zoti abeko katulo ndipo ankaliza mkonono ngati ntchini. Guthera ndi Muriuki anali ata- khala pansi. Guthera anali atakoleka m’khosi mwake kampango ka mwina moyera mwina mwakuda. Zovala zimene Muriuki anavala zinali za zigamba za mitundu yonse imene mugaigan- izire. "Tiyeni tiwadzutse," Guthera anatero. Koma mawu akewa adakali m'kamwa, Matigari anadzuka. "Tiyeni tidzipita," Matigari anatero. Mmene anayankhulira sizinkaoneka n'komwe kuti wangodzuka kumene. "Ndiye tikupita kuti?" anafunsa Muriuki. 212