Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 212
Matigari
Gawo 12
. . . Chilengezo chapadera . . . Apolisi aulula kuti wamisala wina
amene wathawa ndi uja akumadzitchula kuti Matigari ma Njiruungi.
Anthu onse a m'dziko muno akuchenjezedwa kuti asamale ndi mun-
thu ameneyu chifukwa ndi woopsa. Iye akumaganiza kuti chilichonse
ndi chake monga nyumba, malo, mafakitale komanso ngakhale azimayi
onse akuti ndi ake. Aka ndi kachiwiri kuti munthu ameneyu athawe
atamangidwa. Ulendo woyamba anamangidwa pamene ankalimbana
ndi a John Boy Junior pa nkhani ya malo. Iye anauza a Boy kuti akufu-
na makiyi a nyumba yake ndipo ankachita zimenezi mwachiwawa.
Mpaka pano sizinadziwikebe kuti anathawa bwanji kuchokera muselo
limene anatsekeredwa. Kenako anagwidwa n'kupititsidwa kuchipatala
cha anthu amisala dzulo pambuyo ponyoza Nduna Yoona Zachilunga-
mo. Ndunayi imachititsa msonkhano wothetsa mkangano womwe
unachitika pakati pa ogwira ntchito komanso oyendetsa kampani.
Apolisi akufufuzabe kuti chinachitika n'chiyani kuti mzimayi komanso
mnyamata wina aloledwe kulowa m'chipatalachi pataperekedwa
chilengezo kuti amisalawa atsekeredwe kumalo achitetezo chokhwima.
Apolisi akudikirabe mzimayi komanso mnyamatayu kuti apite kupolisi
n'cholinga choti awathandize pakafukufukuyu. Apolisi ena atumizid-
wa kuti apite azikalondera nyumba ya John Boy Junior . . . komanso
John Boy Junior wapatsidwa asilikali omuteteza kwa Matigari ma
Njiruungi . . .
211