Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 211

Matigari Gawo 10 . . . Ino ndi Wailesi Yanu ya Choonadi . . . Apolisi auzidwa kuti asa- mavutitse kapena kugwira azungu omwe sanamete tsitsi komanso nde- vu zawo. Auzidwanso kuti asamawavutitse ngati avala zovala zosaon- eka bwino, akapezeka akuimitsa galimoto kapena ngati alibe ndalama zolipirira basi. Apolisi apereka chilengezo chimenechi boma la United States komanso Britain litadandaula kuti anthu a m'maiko awo akumavutitsidwa akamayenda m'misewu ya m'dziko muno chifukwa anthu akuwaganizira kuti ndi amisala kokha chifukwa choti sanamete ndevu kapena tsitsi lawo. Nduna Yoona Zachilungamo yapepesa mai- kowa ndipo yachenjeza anthu onse kuti asiyiretu mtima watsankho. Anthu onse akuchenjezedwa kuti asamapezere anthu a mitundu ina zifukwa kokha chifukwa chakhungu lawo. Mkulu wa apolisi wauza apolisi komanso anthu onse a m’dziko muno kuti anthu achizungu samapenga misala, zivute zitani. Apolisi akufuna kudziwitsa aliyense kuti anthu amene athawa kuchipatala cha amisala, kupatulapo a m'mayiko achimwenye, onse anali anthu akuda . . . Gawo 11 Tsopano mvetserani chilengezo china chapadera . . . Chilengezo chapadera . . . Apolisi awombera wamisala m'modzi amene anathawa. Apolisi apeza kuti wamisala ameneyu ndi Ngaruro wa Kiriro. Apolisiwo anaona kuti sangachitire mwina koma kumuombera chifu- kwa amaika miyoyo ya ena pangozi. Atamuombera anavulala kwambiri moti anathamangira naye kuchipatala. Asanawomberedwe, anayamba kuthupsa apolisiwo komanso amaopseza kuti ayambitsa zachiwawa. Amanenanso kuti apitirizabe kusokoneza ogwira ntchito kuti azinyan- yala ntchito. Wamisalayu amayesanso kusokoneza apolisiwo ndi ma- ganizo ake oipawo powauza kuti nawonso ndi ogwira ntchito. Anawau- zanso kuti iwowo ali ngati zidole za boma la anthu olemera, eni malo a m’dziko muno komanso ali ngati akazitape a olamulira ankhanza . . . 210