Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 209

Matigari Gawo 6 Mwatsegulayi ndi Wailesi Yanu ya Choonadi . . . Tsopano mvet- serani chilengezo chinanso chochokera kupolisi . . . Apolisi akulimbitsa munthu aliyense amene angaone munthu amene akuyankhula ngati wamisala kuti akanene kupolisi yapafupi. Ayenera kukanena kupolisi akaona munthu amene wavala nsanza ngati wamisala kapena aliyense yemwe sanamete kapena kupesa tsitsi lake. Ayeneranso kukanena ngati ataona munthu aliyense amene akufunsa mafunso osadziwika bwino komanso amene akuchita zinthu zomwe ndi amisala okha omwe amazi- chita. Apolisi anena kuti aliyense yemwe si wamisala ayenera kumeta ndevu komanso tsitsi lake komanso kumavala molongosoka nthawi zonse. Aliyense asayerekeze, tikubwerezanso kuti asayerekeze kuyenda munsewu atavala nsanza chifukwa akhoza kugwidwa . . . Ndiye zinangochitika kuti pamene mayi wina wachikulire komanso mwamuna wake ankatoleza m'mabini ena, anaona chithunzi cha Yesu Khrisu komanso cha Karl Marx. "Anthu odwala omwe akuwalengeza pawailesiwa kuti atha- wa kuchipatala cha amisala aja si awa!" mayiyo anauza mwamuna wake. "Kukhala ngatiditu ndi omwewo! Onsewa ali ndi tsitsi lalita- li komanso ndevu zambiri, ndipo akungooneka ngati akudwala misala!" mwamuna uja anatero. Onse anatenga chithunzi chimodzichimodzi n'kuthamangira nacho kupolisi. "Nyinyi wenda wazimu!"* wapolisi anayankhula mokalipa. " Ife tikufuna amisala enieni, osati zithunzi ayi! Pitani mukafufuze amisala omwe athawa kuchipatala mubwere nawo kuno, kapena ngati mukudziwa kumene ali ingotiperekezani . . . " 208