Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 208
Matigari
Gawo 4
Wansembe uja atangomva zoti amisala athawa kuchipatala,
anabzala maondo ake pansi n'kuyamba kupemphera kwa
Mulungu. “Oh, Ambuye. Simunandipatse mpata woti ndikayen-
dere anthu omwe anali kuchipatala cha anthu amisala . . . Ndiye
ngati mulidi inuyo mwabwera n'kudzionetsa kwa ife ngati mun-
thu wamisala, chonde mudzakumbukire kuti mtumiki wanune
ndimafuna kupita kukawaona mawamawali . . .”
Gawo 5
Ino ndi Wailesi Yanu ya Choonadi . . . Chidziwitso chapadera.
Apolisi akufufuza anthu ena openga omwe athawa kuchokera ku-
chipatala cha anthu amisala. Apolisiwa akufunafunanso mzimayi ko-
manso mnyamata wina, omwe chakum'mawa anapita kuchipatalachi
kukapereka chakudya kwa odwala. Apolisi akupempha mnyamata ko-
manso mayiyo kuti apite kukadzipereka kwa apolisi a m'dera limene
akukhala kuti athandize apolisi kudziwa kumene anthu oopsawa ali, ko-
manso kuti adziwe kuti anathawa bwanji.
207