Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 205

Matigari Gawo 1 Iye anapanga chiganizo chake adakali kuchipatala cha anthu amisala kuja. Ankaona kuti munthu sangagonjetse mdani wake ndi zida zokha, koma ankaonanso kuti munthu sangagonjetse mdani wake ndi mawu okha. Anaona kuti ayenera kukhala ndi mawu oyenerera, komanso kuti mawuwo apatsidwe mphamvu zokwanira bwino ndi zida zankhondo. Kuganizira mmene ana- zunzikira kufunafuna choonadi ndi chilungamo atadzimanga ndi lamba wamtendere kunamupangitsa kusintha maganizo. Anaona kuti chilungamo sichingapezeke ngati munthu atatsatira njira yochita zinthu mwamtendere. Kenako anadziuza kuti: “Pamene wosula zitsulo ankabwerera kwawo atapita koka- kulitsa luso lake, anapeza munthu wina akukhaulitsa mkazi wake yemwe anali woyembekezera. Kodi akanangomupatsa moni munthuyo mwaulemu? Ayi ndithu. Kumeneku kunali ku- mutokosola dala. Iye anayamba kunola mpaliro wake kuti atumbule nawo munthu ankazunza mkazi wakeyo! Inenso an- thu amenewa sindingangowasiyasiya.” “Anthu amene akuponderezedwa amapeza chilungamo kud- zera mumpaliro wonoledwa bwino.” Kenako anachotsa lamba wamtendere uja ndipo anamuponya pansi n'kuyamba kumu- pondaponda. 204